03/06/2025
Wapolisi yemwe amagwira ntchito m'boma la Dedza a Eric Chasweka wadzipha podzimangilira m'nyumba yake.
Mneneri wa apolisi m'chigawo chapakati chakuzambwe, a Foster Benjamin watsimikiza za nkhaniyi kuti a Chasweka anafika ku ntchito komaliza lachisanu ndipo ataweruka sanabwelerenso m'masiku otsatira.
A Benjamin ati izi zinachitsa kuti apolisi anzawo apite kunyumba yake komwe anathyola chitseko chanyumbayi.
Iwo ati anapezaso kalata zauthenga otsanzika kwa mkulu wa polisi ya Dedza, makolo ake komanso bwenzi lake.